Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 106

Matigari kudzachitika chiphwando chokonzekera kubwereranso kunyumba kwathu!” “Kodi mukuganiza kuti mutuluka mwachangu kuno?” anag- widwa akungoyendayenda m’tauni uja anafunsa. “Kubwera kundende kuno ndi kophweka. Koma kuti utuluke pamakhala matatalazi. Ndikukhulupirira kuti mukhalabe muli kuno pofika mawa, mwinanso mpaka tsiku mukunenalo.” “Ndikanakhala kuti sindinayambane ndi bwana komanso wantchito wake, zikanakhalako bwino,” wogwira ntchito uja anatero. Ndazindikira kuti bwana ndi wantchito amenewa san- gasiyane ndipo akhala akutizunza kuyambira kale. Aliyense amadziwa kuti Robert Williams ndi John Boy amangokhala nga- ti ana amapasa omwe anabadwa mimba imodzi n’kuyamwa bere lofanana. Komanso mukudziwa? Apolisi onse m’dziko mu- no ali m’manja mwa anthu amenewa. Ngakhalenso makhoti. Choncho ndikuganiza kuti ungakhale mwayi waukulu ngati mungatuluke mwachangu kuno. Ndithu mvula yamatalala ikho- za kugwa tsiku limenelo. Mungokonzekeretsa maganizo anu kuti muwolera kundende konkuno. Monga mmene mwambi wina uja umanenera, ndende inamangidwira amuna.” “Ngakhalenso azimayi!” wina anawonjezera motero. “Komanso ana.” “Ndi mngelo Gabrieli yekha amene angakutulutseni kuno. Ame!” wamowa uja anatero. Asanamalize kunena mawu amenewa, anamva mtswatswa komanso phokoso lamakiyi mumdima. Mofulumira anazimitsa makandulo aja ndipo onse anakhala chete ataunjikana malo amodzi. 105