Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 105

Matigari “Kodi ukunena kuti ndine kazitape?” munthu uja anauza wokupha munthu uja. “Kodi munamva zoti akazitape amavala zikwangwani pachi- pumi pawo zolembedwa kuti: ‘Onani, ndine kazitape!’” waku- pha munthu uja anayankha. “Aliyense pano akhoza kukhala kazitape wa apolisi.” Zinkangokhala ngati akufuna kubayana ndi mipeni ndipo mipeni yawoyo inkawala ndi kandulo yemwe anali muselolo. “Tasiyani pansi mipeni yanuyo!” Matigari anawalamula ndi mawu amphamvu. “N’chifukwa chiyani mukusolola mipeni kuti mubayane? Kodi mavuto mwapalamulawa sakukukwanira- ni?” Kenako anthu aja anasunga mipeni yawo ija. Ndiyeno mwa- na wasukulu uja anati: “Komatu tilipo anthu asanu ndi m’modzi okha muno. Ndiye sipangakhale kazitape pakati pathu, Yudasi palibe.” Matigari anapitiriza kuyankhula ngati kuti palibe chimene chinachitika. “Mukufuna mudziwe zimene ndikufuna kuchita? Ndikuuza- ni, chifukwa ine sindibisa mawu. Ndabwera kuno nditadziman- ga ndi lamba wamtendere. Mlimi yemwe zomera zake siziku- tuluka samatopa ndi kubzala. Munthu amene akufunafuna chi- lungamo samatopa mpaka atachipeza. Choonadi sichimaola. Choncho choonadi chidzalamulira pangatalike. Ngati si lero ndiye kuti ndi mawa. Nyumba yanga ndi yanga basi. Sikuti ndikufuna kuba ya mwini wake ayi. Ndikungofuna zinthu zom- we ndinamanga ndi manja anga. Mawa ndi tsiku langa. Ndiku- kuitanani nonse kuti mubwere kunyumba kwanga mkucha, ndikunena mawa ndiye tsiku linalo. Mubwere chifukwa 104