Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 103

Matigari “Ukhoza kundifunsa mafunso onse amene uli nawo. Ndikufuna ndikuuzeni, mafunso ndi amene amathandiza mun- thu kukhala wozindikira. Ndilozereni munthu amene safunsa mafunso, kuti ndikulozereni chitsiru. Poyankha funso lako, ndi- nakwirira zida zanga pansi pa mtengo wamkuyu. Kenako ndi- nadzimanga ndi lamba wamtendere. Mumtima mwanga ndina- ti: ‘Tsopano mbendera ndi ya anthu akuda. Choncho kuyambira lero, chilungamo ndi choonadi chithetsa nkhondo zonse; choonadi ndi chilungamo chizithetsa mikangano yonse pakati pa ife anthu akuda. Tiyeni tilole kuti choonadi ndi chilungamo chilamulire dziko.’” “Koma kodi tingadziwe bwanji kuti ndinudi Matigari ma Njiruungi? Tionetseni chizindikiro?” “Wati chizindikiro? . . . Oh, ingodikira pang’ono, uona chi- lungamo chikuyamba kulamulira posachedwapa . . . chifukwa ngati sizitero . . .” Matigari anayankhula mawu amenewa ngati munthu amene wamufunsa kuti kodi Ambuye adzabweranso liti. “Tamvetserani . . . Sindikufunika kuchita chozizwitsa kuti mudziwe kuti ndine ndani. Ntchito za manja anga ndi zimene zingandichitire umboni. Ndivula lamba wamtendereyu n’kuva- la wina wokongoletsedwa ndi zipolopolo m’malo mwa mikan- da. Inde ndiika lamba wazipolopo m’chiunomu n’kunyamula AK47 yanga paphewapa. Kenako ndikaima pamwamba paphiri n’kuuza aliyense kuti: ‘Tsegulani maso kuti muone zimene ine ndaona . . . Tsegulani mapirikaniro anu kuti mumve zimene ine ndamva . . . Lolani kuti zofuna za anthu zichitike! Ufumu wathu ukubwera ngati mmene anachitira abale anthu akale omwe ana- menya nkhondo ya ufulu wawo. Nthaka ndi ya eni ake alimi osati nthata komanso anthu ena ochokera kunja! Choncho kuyambira lero, wolima ayenera kumakolola zimene anafesa; womanga ayenera kumagona m’nyumba; telala ayenera 102