Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Matigari | Page 102
Matigari
“Inde, chilungamo chenicheni ndi champhamvu kuposa lu-
panga. Choonadi chinakopa mlenje wina kuti asalase mdani
wake yemwe ankafuna kumuboola mphafa,” wamowa uja
anatero.
“Koma kodi mwaiwala kuti boma lili ndi Unduna Woona
Zachilungamo?” mwana wa kuyunivesite uja anawakumbutsa
anzakewo.
“Nduna Yoona Zachilungamo ikubwera mawa kuti idzayen-
dere fakitale ija,” wogwira ntchito kufakitale uja anatero.
“Ndiyetu Wofunafuna Choonadi ndi Chilungamo adzafunse
ndunayo kuti choonadi ndi chilungamo chikupezeka kuti,”
mnyamata wa kuyunivesite uja anatero moseka. “Ili ndiye lamu-
lo loyamba: Usatchule dzina la choonadi ndi chilungamo pacha-
be.”
“Odi ine nditseke pakamwa panga kuti ndisapalamulenso
mavuto ena!” wakuba nsima uja anatero. “Kodi awa si aphunz-
itsi? Kodi posachedwapa ananena kuti amangidwa chifukwa
chiyani? Anati abwera kuno chifukwa cha pakamwa. Nanga
bwanji mwana wasukuluyu? Nayenso chimodzimodzi. Akulu
anati ukayenda siya phazi, ukasiya pakamwa pamakutsata!”
“Nanunso tiuzeni chimene chachitika kuti mupezeke kuno,”
mwana wa kuyunivesite uja anatero.
Onse anayamba kuseka. Munthu anali asanayankhule uja
anatsukuluza kukhosi kwake. Kenako anayamba kuyankhula
ndi Matigari kuti: “Kodi ndingakufunseniko funso limodzi?
Mwanena kuti mwabwera kuchokera kunkhalango lero
m’mawawu. Kodi zida zanu zili kuti? Kapena munali muli nazo
pamene amakumangani?”
101